Pitani ku nkhani yake

Pitani ku mitu ya nkhani

Tikufunikira Dziko Labwino

Tikufunikira Dziko Labwino

A António Guterres omwe ndi mlembi wamkulu wa bungwe la United Nations ananena kuti: “Tikukhala m’dziko lodzaza ndi mavuto.” Kodi inunso mukuona choncho?

Nkhani zimene timamvetsera, kuonera ndi kuwerenga, zimakhala ndi zinthu zambiri zodetsa nkhawa monga:

  • Matenda ndi miliri

  • Ngozi za m’chilengedwe

  • Umphawi ndi njala

  • Kuonongeka kwa mpweya ndi madzi komanso kutentha kwa dziko

  • Kuphwanya malamulo, zachiwawa ndiponso zachinyengo

  • Nkhondo

Mpake kuti tikufunikira dziko labwino. Dziko limene mudzakhale

  • Anthu athanzi labwino

  • Chitetezo

  • Chakudya chokwanira

  • Mpweya ndi madzi abwino

  • Chilungamo chenicheni

  • Mtendere wochuluka

Kodi tikamanena kuti dziko labwino tikutanthauza chiyani?

Kodi n’chiyani chimene chidzachitikire dziko limene tikukhalamoli?

Kodi tingatani kuti tidzakhale m’dziko labwino?

Magaziniyi ifotokoza mayankho otonthoza ochokera m’Baibulo a mafunso amenewa ndi enanso.