Pitani ku nkhani yake

Pitani ku mitu ya nkhani

Kodi Mungayankhe Bwanji?

Kodi Mungayankhe Bwanji?

Kodi Mungayankhe Bwanji?

Kodi N’chiyani Chikusowa Pachithunzichi?

Werengani Machitidwe 10:9-48. Ndiyeno onani chithunzichi. N’chiyani chikusowapo? Lembani mayankho anu m’mizere ili munsiyi ndipo malizitsani kujambula chithunzichi.

1. ․․․․․

2. ․․․․․

3. ․․․․․

KAMBIRANANI:

Kodi mukuganiza kuti Yehova ankafuna kumuphunzitsa Petulo chiyani?

ZOKUTHANDIZANI: Werengani Machitidwe 10:28, 34, 35.

Mukakhala ndi anthu a mitundu ina, kodi mungasonyeze bwanji kuti mwaphunzirapo kanthu pa nkhani ya Petulo imeneyi?

Zithunzi Zoti Ana Apeze

Kodi mungathe kupeza zithunzi izi m’magazini ino? Fotokozani zimene zikuchitika pa chithunzi chilichonse.

Kuchokera M’magazini Ino

Yankhani mafunso omwe ali m’munsiwa, ndipo lembani vesi kapena mavesi a m’Baibulo omwe akusowapo.

TSAMBA 9 Kodi anthu sangathe kuzindikira chiyani? Mlaliki 3:․․․

TSAMBA 10 Kodi dziko lapansi linaperekedwa kwa ndani? Salmo 115:․․․

TSAMBA 13 Kodi tiyenera kuzindikira chiyani kuti tikhale osangalala? Mateyo 5:․․․

TSAMBA 19 Kodi zolingalira zimazimidwa popanda chiyani? Miyambo 15:․․․

Kodi N’chiyani Chimene Mukudziwa Chokhudza Woweruza Samsoni?

Werengani Oweruza 13:1–16:31. Ndiyeno yankhani mafunso otsatirawa.

4. ․․․․․

Kodi iye anali wochokera fuko liti?

5. ․․․․․

Anapulumutsa Aisiraeli kwa anthu a mtundu uti?

6. ․․․․․

Zoona kapena zonama? Iye anakhala ndi moyo mneneri Samueli atafa.

KAMBIRANANI:

N’chifukwa chiyani Samsoni anali wamphamvu kwambiri?

ZOKUTHANDIZANI: Werengani Aheberi 11:32-34. Kodi ndi zochitika ziti za m’nkhani ya Samsoni zimene munasangalala nazo kwambiri, nanga n’chifukwa chiyani?

▪ Mayankho ali patsamba  22

MAYANKHO A MAFUNSO A PATSAMBA 31

1. Palibe nyama za miyendo inayi.

2. Palibe nyama zokwawa.

3. Palibe mbalame.

4. Dani.—Oweruza 13:2-5.

5. Afilisiti.—Oweruza 13:1.

6. Zonama.