Yeremiya 46:1-28

  • Ulosi wokhudza Iguputo (1-26)

    • Iguputo adzagonjetsedwa ndi Nebukadinezara (13, 26)

  • Zimene Aisiraeli analonjezedwa (27, 28)

46  Awa ndi mawu amene Yehova anauza mneneri Yeremiya okhudza mitundu ya anthu:+  Uwu ndi uthenga wokhudza Iguputo+ wonena za gulu la asilikali a Farao Neko,+ mfumu ya Iguputo, amene anagonjetsedwa ndi Nebukadinezara* mfumu ya Babulo ku Karikemisi, mʼmbali mwa mtsinje wa Firate. Anagonjetsedwa ndi mfumu imeneyi mʼchaka cha 4 cha ulamuliro wa Yehoyakimu+ mwana wa Yosiya, mfumu ya Yuda. Uthengawo unali wakuti:   “Tengani zishango zanu zazingʼono ndi zazikulu,Ndipo mupite kukamenya nkhondo.   Inu okwera pamahatchi, mangani mahatchi anu nʼkukwerapo. Valani zipewa zanu ndipo mukonzeke. Pukutani mikondo yanu ingʼonoingʼono ndipo muvale zovala zanu zamamba achitsulo.   ‘Nʼchifukwa chiyani akuoneka kuti agwidwa ndi mantha? Akubwerera ndipo asilikali awo agonjetsedwa. Iwo athawa mwamantha ndipo asilikali awo sanacheuke. Zochititsa mantha zili paliponse,’ akutero Yehova.   ‘Munthu waliwiro komanso asilikali sangathe kuthawa. Iwo apunthwa nʼkugwa.Zimenezi zachitikira kumpoto mʼmphepete mwa mtsinje wa Firate.’+   Kodi uyu amene akubwera ngati mtsinje wa Nailo,Kapena ngati mitsinje ya madzi amphamvu, ndi ndani?   Dziko la Iguputo likubwera ngati mtsinje wa Nailo,+Likubwera ngati mitsinje ya madzi amphamvu,Ndipo likunena kuti, ‘Ndipita kukaphimba dziko lapansi. Ndikawononga mzinda ndi onse amene akukhala mumzindawo.’   Inu mahatchi pitani. Inu magaleta thamangani ndi liwiro lalikulu! Lolani asilikali kuti apite.Lolani Kusi ndi Puti amene amadziwa kugwiritsa ntchito chishango kuti apite,+Komanso anthu a ku Ludimu+ amene amadziwa kukunga ndi kuponya uta.+ 10  “Limeneli ndi tsiku la Yehova wa magulu ankhondo akumwamba, Ambuye Wamkulu Koposa ndipo ndi tsiku lobwezera chilango kwa adani ake. Lupanga lidzadya adaniwo nʼkukhuta ndipo lidzamwa magazi awo mpaka ludzu lake litatha. Zimenezi zidzachitika chifukwa Yehova wa magulu ankhondo akumwamba, Ambuye Wamkulu Koposa, ali ndi nsembe imene akufuna kupereka mʼdziko lakumpoto, mʼmphepete mwa mtsinje wa Firate.+ 11  Iwe namwali, mwana wamkazi wa Iguputo,Pita ku Giliyadi kuti ukatenge mafuta a basamu.+ Wachulukitsa njira zochiritsira zimene sizinakuthandize,Chifukwa sunachiritsidwe.+ 12  Mitundu ya anthu yamva zochititsa manyazi zimene zakuchitikira,+Ndipo kulira kwako kwamveka mʼdziko lonse. Asilikali apunthwitsana,Ndipo onse agwera limodzi.” 13  Yehova anauza mneneri Yeremiya zokhudza kubwera kwa Nebukadinezara* mfumu ya Babulo kudzaukira dziko la Iguputo. Iye anati:+ 14  “Lengezani zimenezi mu Iguputo, muzilengeze ku Migidoli.+ Lengezani zimenezi ku Nofi* ndi ku Tahapanesi.+ Munene kuti, ‘Imani mʼmalo anu ndipo mukhale okonzeka,Chifukwa lupanga lidzawononga anthu onse amene akuzungulirani. 15  Nʼchifukwa chiyani amuna anu amphamvu akokoloka? Iwo sanathe kulimba,Chifukwa Yehova wawagonjetsa. 16  Ambiri akupunthwa ndi kugwa. Iwo akuuzana kuti: “Imirirani, tiyeni tibwerere kwa anthu a mtundu wathu ndi kudziko lathuChifukwa takumana ndi lupanga loopsa.”’ 17  Kumeneko asilikali anu akunena kuti,‘Farao mfumu ya Iguputo akungoopseza ndi pakamwa chabeNdipo wataya mwayi.’*+ 18  ‘Pali ine Mulungu wamoyo,’ yatero Mfumu, imene dzina lake ndi Yehova wa magulu ankhondo akumwamba,‘Iye* adzabwera nʼkuonekera ngati phiri la Tabori+ pakati pa mapiri enaNdiponso ngati phiri la Karimeli+ mʼmphepete mwa nyanja. 19  Longedza katundu wako pokonzekera kupita ku ukapolo,Iwe mwana wamkazi amene ukukhala mu Iguputo. Chifukwa mzinda wa Nofi* udzakhala chinthu chochititsa mantha.Udzawotchedwa ndi moto* ndipo simudzapezeka aliyense wokhalamo.+ 20  Iguputo ali ngati ngʼombe yaikazi yooneka bwino imene sinaberekepo,Koma ntchentche zoluma zidzabwera kuchokera kumpoto kudzamuwononga. 21  Ngakhale asilikali amene wawalemba ganyu ali ngati ana a ngʼombe onenepa,Koma iwonso abwerera ndipo onse athawa. Sanathe kulimba,+Chifukwa tsiku la tsoka lawo lafika,Nthawi yoti aweruzidwe yakwana.’ 22  ‘Iye akuchita phokoso ngati la njoka imene ikuthamanga,Chifukwa adaniwo amufikira mwamphamvu, atatenga nkhwangwa,Ngati amuna amene akukagwetsa mitengo.* 23  Iwo adzadula nkhalango yake ngakhale kuti ndi yowirira,’ akutero Yehova. ‘Chifukwa adaniwo ndi ochuluka kwambiri kuposa dzombe ndipo ndi osawerengeka. 24  Mwana wamkazi wa Iguputo adzachititsidwa manyazi. Iye adzaperekedwa mʼmanja mwa anthu akumpoto.’+ 25  Yehova wa magulu ankhondo akumwamba, Mulungu wa Isiraeli, wanena kuti: ‘Tsopano ndilanga Amoni+ wa ku No,*+ Farao, Iguputo pamodzi ndi milungu yake+ ndi mafumu ake. Inde ndilanga Farao ndi onse amene amamukhulupirira.’+ 26  ‘Ndidzapereka anthu a ku Iguputo mʼmanja mwa anthu amene akufuna moyo wawo, mʼmanja mwa Nebukadinezara* mfumu ya Babulo+ ndi mʼmanja mwa atumiki ake. Koma kenako anthu adzakhalanso mʼdzikolo ngati mmene zinalili kale,’ akutero Yehova.+ 27  ‘Koma iwe Yakobo mtumiki wanga, usaopeNdipo usachite mantha, iwe Isiraeli.+ Chifukwa ndidzakupulumutsa kuchokera kutali.Ndipo ndidzapulumutsa mbadwa* yako kuchokera mʼdziko limene anali kapolo.+ Yakobo adzabwerera nʼkukhala mwamtendere ndiponso mosatekeseka,Sipadzakhala wowaopseza.+ 28  Choncho, iwe Yakobo mtumiki wanga usachite mantha, chifukwa ine ndili ndi iwe. Ndidzawononga anthu a mitundu yonse kumene ndakubalalitsirako,+Koma iwe sindidzakuwononga.+ Ndidzakulanga* pamlingo woyenera,+Ndipo sindidzakusiya osakupatsa chilango,’ akutero Yehova.”

Mawu a M'munsi

Mʼchilankhulo choyambirira, “Nebukadirezara.” Kameneka ndi kalembedwe kena ka dzinali.
Mʼchilankhulo choyambirira, “Nebukadirezara.” Kameneka ndi kalembedwe kena ka dzinali.
Kapena kuti, “ku Memfisi.”
Mʼchilankhulo choyambirira, “wataya nthawi imene anasankhiratu.”
Kutanthauza amene adzagonjetse Iguputo.
Kapena kuti, “Memfisi.”
Mabaibulo ena amati, “Udzasanduka bwinja.”
Kapena kuti, “amene akukatola nkhuni.”
Amene ndi Thebesi.
Mʼchilankhulo choyambirira, “Nebukadirezara.” Kameneka ndi kalembedwe kena ka dzinali.
Mʼchilankhulo choyambirira, “mbewu.”
Kapena kuti, “Ndidzakulangiza.”