Pitani ku nkhani yake

Pitani ku mitu ya nkhani

FUNSO 15

Kodi Mungatani Kuti Muzikhala Osangalala?

“Ndi bwino kudya zamasamba koma pali chikondi, kusiyana ndi kudya nyama ya ngʼombe yamphongo yonenepa koma pali chidani.”

Miyambo 15:17

“Ine Yehova ndine Mulungu wanu, amene ndimakuphunzitsani kuti zinthu zikuyendereni bwino, amene ndimakutsogolerani mʼnjira imene mukuyenera kuyenda.”

Yesaya 48:17

“Osangalala ndi anthu amene amazindikira zosowa zawo zauzimu chifukwa Ufumu wakumwamba ndi wawo.”

Mateyu 5:3

“Uzikonda mnzako mmene umadzikondera wekha.”

Mateyu 22:39

“Zimene mukufuna kuti anthu akuchitireni, inunso muwachitire zomwezo.”

Luka 6:31

“Osangalala ndi anthu amene akumva mawu a Mulungu nʼkuwasunga.”

Luka 11:28

“Ngakhale munthu atakhala ndi zochuluka chotani, moyo wake suchokera mʼzinthu zimene ali nazo.”

Luka 12:15

“Choncho, ngati tili ndi chakudya, zovala ndi pogona, tizikhala okhutira ndi zinthu zimenezi.”

1 Timoteyo 6:8

“Kupatsa kumatichititsa kukhala osangalala kwambiri kuposa kulandira.”

Machitidwe 20:35