Pitani ku nkhani yake

Kodi Mungatani Kuti Musamaope Kwambiri Imfa?

Kodi Mungatani Kuti Musamaope Kwambiri Imfa?

Yankho la m’Baibulo

 N’zoona kuti timaopa imfa popeza ndi mdani wathu ndipo timayesetsa kuchita zinthu zoyenerera zotetezera moyo wathu. (1 Akorinto 15:26) Koma anthu ena amaopa kwambiri imfa chifukwa amakhulupirira zinthu zabodza kapena mizimu, ndipo zimenezi zimawachititsa kuti akhale “mu ukapolo moyo wawo wonse.” (Aheberi 2:15) Choncho munthu akadziwa zoona zake pa nkhaniyi, saopa kwambiri imfa ndipo zimenezi zingamuthandize kuti azisangalala ndi moyo.​—Yohane 8:32.

Zoona zake zokhudza imfa

  •   Anthu akufa sadziwa kanthu. (Salimo 146:4) Simukuyenera kuopa kuti mukadzamwalira muzikazunzika chifukwa Baibulo limayerekezera imfa ndi tulo.​​—Salimo 13:3; Yohane 11:​11-14.

  •   Anthu akufa sangativulaze. Ngakhale anthu amene anali okonda zachiwawa pamene anali ndi moyo, akamwalira amakhala “anthu akufa.” (Miyambo 21:16) Baibulo limati “chidani chawo ndiponso nsanje yawo zatha kale.”​—Mlaliki 9:6.

  •   Sikuti munthu aliyense akamwalira ndiye kuti zake zathera pomwepo. Mulungu adzaukitsa anthu amene anamwalira.​—Yohane 5:​28, 29; Machitidwe 24:15.

  •   Mulungu akulonjeza nthawi imene “imfa sidzakhalaponso.” (Chivumbulutso 21:4) Ponena za nthawi imeneyo, Baibulo limati: “Olungama adzalandira dziko lapansi, ndipo adzakhala mmenemo kwamuyaya.” Iwo sadzaopanso ngakhale pang’ono kuti mwina akhoza kufa.​—Salimo 37:29.