Pitani ku nkhani yake

Kodi Ndizipemphera kwa Anthu Oyera Mtima?

Kodi Ndizipemphera kwa Anthu Oyera Mtima?

Yankho la m’Baibulo

 Ayi. Baibulo limatiuza kuti tizipemphera kwa Mulungu yekha, m’dzina la Yesu. Yesu anauza ophunzira ake kuti: “Chifukwa chake pempherani inu chomwechi: Atate wathu wa Kumwamba, Dzina lanu liyeretsedwe.” (Mateyu 6:9, Buku Lopatulika Ndilo Mau a Mulungu) Yesu anauza ophunzira ake kuti azipemphera kwa Mulungu yekha, osati kwa anthu oyera mtima, angelo kapena wina aliyense.

 Yesu anauzanso otsatira ake kuti: “Ine ndine njira, ndi choonadi, ndi moyo. Palibe munthu adza kwa Atate, koma mwa Ine.” (Yohane 14:6, Buku Lopatulika Ndilo Mau a Mulungu) Mulungu anapereka udindo kwa Yesu yekha woti azitichonderera kwa iye.—Aheberi 7:25.

Kodi pali vuto ngati nditamapemphera kwa Mulungu komanso kwa anthu oyera mtima?

 Mulungu anapatsa anthu ake Malamulo Khumi. M’lamulo lina, iye ananena kuti: “Ine Yehova Mulungu wako ndiri Mulungu wansanje.” (Ekisodo 20:5, Buku Lopatulika Ndilo Mau a Mulungu) Kodi mawu akuti Yehova ndi “Mulungu wansanje” akutanthauza chiyani? Mawu a m’munsi palembali mu Baibulo la Dziko Latsopano amanena kuti iye ndi “Mulungu wosalola aliyense kupikisana naye.” Mulungu amafuna kuti anthu azilambira ndiponso kupemphera kwa iye yekha.—Yesaya 48:11.

 Mulungu sasangalala tikamapemphera kwa milungu ina kapena anthu ena, ngakhale kwa anthu oyera mtima kapenanso angelo. Pa nthawi ina, mtumwi Yohane ankafuna kulambira mngelo, koma mngeloyo anamuletsa n’kumuuza kuti: “Usatero; ine ndine kapolo mnzako, ndi mnzawo wa abale ako akukhala nawo umboni wa Yesu; lambira Mulungu.”—Chivumbulutso 19:10, Buku Lopatulika Ndilo Mau a Mulungu.