Pitani ku nkhani yake

A Mboni za Yehova Amaphunzitsa Makolo ndi Ana Mmene Angapewere Anthu Ogwiririra Ana

A Mboni za Yehova Amaphunzitsa Makolo ndi Ana Mmene Angapewere Anthu Ogwiririra Ana

Baibulo limanena kuti makolo ayenera kukonda ana awo, kuwatsogolera, kuwateteza komanso kumawaona kuti ndi mphatso imene Mulungu anawapatsa. (Salimo 127:3; Miyambo 1:8; Aefeso 6:1-4) Masiku ano kukuchitika zinthu zoopsa zambiri monga kugwiririra ana. Choncho makolo ayenera kuyesetsa kuteteza ana awo kwa anthu oterewa.

Kwa zaka zambiri, a Mboni za Yehova akhala akulemba komanso kufalitsa nkhani zimene zimathandiza kuti aliyense azisangalala m’banja. Akhalanso akutulutsa nkhani zimene zimathandiza makolo kuteteza ana awo kwa achidyamakanda komanso kuwaphunzitsa zokhudza anthu ogwiririra ana. M’munsimu muli zina mwa nkhani zimene a Mboni za Yehova atulutsapo zimene zili ndi malangizo othandiza okhudza kuteteza ana kwa achidyamakanda. Tasonyezanso kuchuluka kwa magazini ndi mabuku komanso zinenero zimene nkhanizi zinatulutsidwa. *

A Mboni za Yehova apitiriza kuphunzitsa makolo ndi ana awo kuti atetezeke kwa anthu ogwiririra.

^ ndime 3 Chaka chimene tasonyeza ndi chomwe nkhanizo zinatuluka m’Chingelezi.