Pitani ku nkhani yake

Pitani ku mitu ya nkhani

NYIMBO 90

Tizilimbikitsana

Tizilimbikitsana

(Aheberi 10:​24, 25)

  1. 1. Pomwe tikulimbikitsana

    Kutumikira Yehova,

    Chikondi chathu chimakula

    Ndipo timagwirizana.

    Chikondi cha anthu a M’lungu

    N’chothandiza kupirira.

    Timatetezedwa kwambiri

    Tikamakhala mumpingo.

  2. 2. Mawu a pa nthawi yabwino

    Amatilimbikitsadi.

    Mawu otilimbikitsawa

    Amachoka kwa abale.

    Kugwirira ntchito limodzi

    Kumatigwirizanitsa.

    Tizikhala olimbikitsa

    Ndipo tizithandizana.

  3. 3. Pamene tsiku la Yehova

    Layandikira kwambiri,

    Tipitirize kusonkhana

    Kuti tiyende ndi M’lungu.

    Tigwirizane ndi abale,

    Titumikire limodzi.

    Choncho tizilimbikitsana

    Kuti tikhulupirike.