Pitani ku nkhani yake

Pitani ku mitu ya nkhani

NYIMBO 76

Kodi Mumamva Bwanji?

Kodi Mumamva Bwanji?

(Aheberi 13:15)

  1. 1. Kodi m’mamva bwanji

    Mukasonyeza khama

    Polalikira anthu

    Ndi kuwaphunzitsa?

    Mukamayesetsa

    M’lungu adzadalitsa.

    Mudzathandiza anthu

    Kudziwa Mulungu.

    (KOLASI)

    Timasangalala ndithu

    Kupereka mtima wathu,

    Choncho timutumikire

    Tsiku lililonse.

  2. 2. Kodi m’mamva bwanji

    Mukadziwatu kuti

    Mwawafika pamtima

    Akamva uthenga?

    Ena amakana,

    Ena amatitsutsa.

    Koma timanyadira

    Tikalalikira.

    (KOLASI)

    Timasangalala ndithu

    Kupereka mtima wathu,

    Choncho timutumikire

    Tsiku lililonse.

  3. 3. Kodi m’mamva bwanji

    Pokumbukira kuti

    Mwa chikondi Yehova

    Amatsogolera?

    Timalalikira,

    Timaphunzitsa anthu

    Akhale ndi tsogolo,

    Adzapeze moyo.

    (KOLASI)

    Timasangalala ndithu

    Kupereka mtima wathu,

    Choncho timutumikire

    Tsiku lililonse.