NYIMBO 23
Yehova Wayamba Kulamulira
-
1. Ufumu wa Mulungu
ukulamuliradi.
Khristu ndiye mwala mu Ziyoni.
Tonse tikweze mawu,
tiimbire Mulungu.
Yesu wakhala pa
Mpando wachifumu.
(KOLASI)
Ufumu ubweretsa chani?
Chilungamo, choonadi.
Udzabweretsanso chiyani?
Moyo wosatha padziko.
Tamandani Yesu Mfumu,
Iye ndi wachikondi.
-
2. Khristu ali pampando.
Amagedo ifika
Kudzawononga anthu oipa.
Choncho tilalikire
kuti ambiri amve
Ndipo ofatsa abwere
kwa Mulungu.
(KOLASI)
Ufumu ubweretsa chani?
Chilungamo, choonadi.
Udzabweretsanso chiyani?
Moyo wosatha padziko.
Tamandani Yesu Mfumu,
Iye ndi wachikondi.
-
3. Tilemekeze Mfumu
yomwe ndi yachikondi.
Yatumidwa ndi Yehova M’lungu.
Tizipempha Yehova
kuti atithandize,
Chifukwa oipa
adzawonongedwa.
(KOLASI)
Ufumu ubweretsa chani?
Chilungamo, choonadi.
Udzabweretsanso chiyani?
Moyo wosatha padziko.
Tamandani Yesu Mfumu,
Iye ndi wachikondi.
(Onaninso 2 Sam. 7:22; Dan. 2:44; Chiv. 7:15.)