NYIMBO 150
Bwerani kwa Mulungu Kuti Mupulumuke
-
1. Mitundu ya anthu
Ikutsutsabe Yesu.
Ulamuliro wa anthu
Utha watero M’lungu.
Ufumu wa M’lungu
Ukulamuliradi.
Yesu adzachotsa adani.
Adzatha posachedwa.
(KOLASI)
Bweranitu kwa Yehova
Kuti mudzapulumuke.
Musakayike,
Muzimumvera,
Mukhale kumbali yake.
Adzakupulumutsani
Ndi mphamvu zake.
-
2. Anthu akusankha
Kumvetsera uthenga.
Timalalikira onse.
Enatu amakana.
Tikamavutika
Tisakhale ndi mantha.
M’lungu adzatisamalira
Timukhulupirire.
(KOLASI)
Bweranitu kwa Yehova
Kuti mudzapulumuke.
Musakayike,
Muzimumvera,
Mukhale kumbali yake.
Adzakupulumutsani
Ndi mphamvu zake.
(Onaninso 1 Sam. 2:9; Sal. 2:2, 3, 9; Miy. 2:8; Mat. 6:33.)