NYIMBO 115
Tizithokoza Kuleza Mtima kwa Mulungu
-
1. Yehova Mulungu wamphamvu
Mumakonda chilungamo.
Ngakhale zoipa m’dziko
Zikungochulukirabe,
Tikudziwa simukuchedwa
Posachedwa mudzazichotsa.
(KOLASI)
Tikudikira mwachidwi.
Timatamanda dzina lanu.
-
2. Zaka zambiritu kwa inu
Ndi nthawi yochepa chabe.
Tsiku lanu lalikulu
Layandikira kwambiri.
Anthu ochimwa akalapa
Mumasangalala kwambiri.
(KOLASI)
Tikudikira mwachidwi.
Timatamanda dzina lanu.
(Onaninso Neh. 9:30; Luka 15:7; 2 Pet. 3:8, 9.)