Pitani ku nkhani yake

Pitani ku mitu ya nkhani

Esitere Anali Wolimba Mtima

Esitere Anali Wolimba Mtima

Pangani Dawunilodi:

  1. 1. Anali wamasiye

    Komanso kapolo.

    Anaphunzira za M’lungu

    Kwa Moredekai.

    Zinthu zinasintha,

    N’kukhala mfumukazi.

    Sanakane, anamvera.

    Nane ndimvere.

    (KOLASI)

    Esitere anali

    Mkazi wolimba mtima.

    Anamveratu Yehova.

    N’chitsanzo chabwino.

    Anadalira M’lungu,

    Anadalitsidwanso.

    Nane ndim’tsanzira,

    Ndidzilimba mtima.

  2. 2. Mfumu inkamukonda,

    Anali wabwino.

    Anali waulemu,

    Anali wanzeru.

    Anatetezatu,

    Mtundu wake usaphedwe.

    Sanakane, anamvera.

    Nane ndimvere.

    (KOLASI)

    Esitere anali

    Mkazi wolimba mtima.

    Anamveratu Yehova.

    N’chitsanzo chabwino.

    Anadalira M’lungu,

    Anadalitsidwanso.

    Nane ndim’tsanzira

    Ndidzilimba mtima. Mukhale wolimba mtima ngati Esitere.