Onani zimene zilipo

Onani nkhani zake

Limba, Khala na Mphamvu

Limba, Khala na Mphamvu

Daunilodi:

  1. 1. Pali mdima panja apa.

    Conco apemphela

    Za ana ake na za abale

    Kuti alimbe mtima.

    Zinthu zikavuta

    Samabwelela mumbuyo.

    Pali nyimbo amakonda

    Imamulimbitsa.

    (KOLASI)

    “N’dzakulimbitsa

    Usayope

    Nili na iwe,

    N’dzakuthandiza,

    Iwe limba mtima.”

    Akonda Nyimboyi.

    “Adzakulimbitsa

    Nokupatsa mphamvu.”

    (BILIJI)

    Nthawi yosakilila

    Banja zofunika,

    Kaya ziyende bwanji?

    Mabwenzi samulekelela, conco,

    Iye sadela nkhawa.

  2. 2. Adzakalanso na mphamvu,

    Monga ni mbalame.

    Asamalila zonse za pabanja.

    Apemphela ca mumtima.

    Ni olema kwambili.

    Ayetsetsadi mwamphamvu,

    Koma pali nyimbo akonda

    Imamulimbitsa.

    (KOLASI)

    “N’dzakulimbitsa

    Usayope

    Nili na iwe,

    N’dzakuthandiza,

    Iwe limba mtima.”

    Akonda Nyimboyi.

    “Adzakulimbitsa

    Nokupatsa mphamvu.

    Adzakulimbitsa

    Nokupatsa mphamvu.”