NYIMBO 96
Buku lake la Mulungu ni Cuma
(Miyambo 2:1)
-
1. Pali buku limene mau ake,
Tikaŵelenga timakondwela.
Mfundo zake zodabwitsa n’zamphamvu;
Zimatipatsa ciyembekezo.
Bukulo ndilo Baibo yoyela
Analemba anauzilidwa.
Anali amuna okonda M’lungu.
Analemba mwa mphamvu ya mzimu.
-
2. Analemba nkhani za cilengedwe,
Mmene M’lungu anacipangila.
Analemba za moyo m’paradaiso
Komanso mmene unasinthila.
Analemba za mngelo wina wake
Amene anatsutsa Yehova.
Izi zinabweletsadi mavuto
Koma Yehova adzapambana.
-
3. Lomba yafika nthawi tikondwele,
Yesu wayamba kulamulila.
Tilalikile uthenga wabwino
Wonena za Ufumu wa M’lungu.
M’buku lake muli zosangalatsa;
Mulidi cakudya coculuka.
Limatipatsa mtendele wambili.
Tifunika tiziliŵelenga.
(Onaninso 2 Tim. 3:16; 2 Pet. 1:21.)