NYIMBO 118
“Tiwonjezeleni Cikhulupililo”
(Luka 17:5)
-
1. O Yehova, ise ndise ocimwa,
Mtima wathu ‘mafuna zoipa.
Nthawi zina ise zimativuta
Kukhala na cikhulupililo.
(KOLASI)
O Yehova, ise tikupemphani
Kuti mumvele pemphelo lathu.
M’tiwonjezele cikhulupililo,
Kuti’se tikulemekezeni.
-
2. Ngati tilibe cikhulupililo
N’covuta kukukondweletsani.
Koma ngati timakhulupilila,
Tidzatumikila mosaopa.
(KOLASI)
O Yehova, ise tikupemphani
Kuti mumvele pemphelo lathu.
M’tiwonjezele cikhulupililo,
Kuti’se tikulemekezeni.
(Onaninso Gen. 8:21; Aheb. 11:6; 12:1.)